Maphunziro a Lamulo lokhudza ukwati ndi maubale a pabanja ndi anthu a kwa Chinsapo ku Lilongwe
Tinali ku Chinsapo Primary School kumene timakumana ndi a Citizen Forum kuchokera ku Bwaila komanso Kampuno constituences, ku Lilongwe City. Nkhani imene inamanga nthenje kumeneku ndi ya kuphunzitsa lamulo lowona za ukwati, mabanja ndi kutha kwa ukwati komanso lamulo logawa ndi kuteteteza chuma cha masiye. Ku msonkhanowu, anthu anapatsidwa mwayi ofunsa mafunso pa nkhanizi ndipo ife a Malawi Law Commission tinayankha mafunso onse. Ntchitoyi tinayigwira ndi amzathu aku NICE Public Trust Malawi komanso Department of Civic Education.
